Masalimo 70
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho.
70 Fulumirani Mulungu kundipulumutsa;
Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Iwo amene akufunafuna moyo wanga
achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene akukhumba chiwonongeko changa
abwezedwe mopanda ulemu.
3 Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,”
abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 Koma onse amene akufunafuna Inu
akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 Koma ine ndine wosauka ndi wosowa;
bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu.
Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga;
Inu Yehova musachedwe.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.